Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 4:19-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Koma Petro ndi Yohane anayankha nati kwa iwo, Weruzani, ngati nkwabwino pamaso pa Mulungu kumvera inu koposa Mulungu;

20. pakuti sitingatheife kuleka kulankhula zimene tinaziona ndi kuzimva.

21. Koma m'mene anawaopsanso anawamasula, osapeza kanthu kakuwalanga, cifukwa ca anthu; pakuti onse analemekeza Mulungu cifukwa ca comwe cidacitika.

22. Pakuti anali wa zaka zace zoposa makumi anai munthuyo, amene cizindikilo ici cakumciritsa cidacitidwa kwa iye.

23. Ndipo m'mene anamasulidwa, anadza kwa anzao a iwo okha, nawauza ziri zonse oweruza ndi akulu adanena nao.

24. Ndipo m'mene adamva, anakweza mau kwa Mulungu ndi mtima umodzi, nati, Mfumu, Inu ndinu wolenga thambo la kumwamba ndi dziko, ndi nyanja, ndi zonse ziri m'menemo;

25. amene mwa Mzimu Woyera, pakamwa pa kholo lathu Davine mtumiki wanu, mudati,Amitundu anasokosera cifukwaciani?Nalingirira zopanda pace anthu?

26. Anadzindandalitsa mafumu a dziko,Ndipo oweruza anasonkhanidwa pamodzi,Kutsutsana ndi Ambuye, ndi Kristu wace.

27. Pakuti zoonadi anasonkhanidwa m'mudzi muno Herode, ndi Pontiyo Pilato yemwe pamodzi ndi amitundu ndi anthu a Israyeli kumcitira coipa Mwana wanu wopatulika Yesu amene munamdzoza;

28. kuti acite ziri zonse dzanja lanu ndi uphungu wanu zidaweruziratu zicitike.

29. Ndipo tsopano Ambuye, penyani mau ao akuopsa, ndipo patsani kwa akapolo anu alankhule mau anu ndi kulimbika mtima konse,

30. m'mene mutambasula dzanja lanu kukaciritsa; ndi kuti zizindikilo ndi zozizwa zicitidwe mwa dzina la Mwana wanu wopatulika Yesu.

31. Ndipo m'mene adapemphera iwo, panagwedezeka pamalo pamene adasonkhanirapo; ndipo anadzazidwa onse ndi Mzimu Woyera, nalankhula mau a Mulungu molimbika mtima.

32. Ndipo unyinji wa iwo akukhulupira anali wa mtima umodzi ndi moyo umodzi; ndipo sananena mmodzi kuti kanthu ka cuma anali naco ndi kace ka iye yekha; koma anali nazo zonse zodyerana.

33. Ndipo atumwi anacita umboni ndi mphamvu yaikulu za kuuka kwa Ambuye Yesu; ndipo panali cisomo cacikuru pa iwo onse.

34. Pakuti mwa iwo munalibe wosowa; 1 pakuti onse amene anali nayo minda, kapena nyumba, anazigulitsa nabwera nao malonda ace a izo adazigulitsa,

35. 2 nawaika pa mapazi a atumwi; ndipo anagawira yense monga kusowakwace.

36. Ndipo Yosefe, wochedwa ndi atumwi Bamaba (ndilo losandulika mwana wa cisangalalo), Mlevi, pfuko lace la ku Kupro,

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 4