Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 4:13-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Koma pakuona kulimbika mtima kwa Petro ndi Yohane, ndipo pozindikira kuti ndiwo anthu osaphunzira ndi opulukira, anazizwa ndipo anawazindikira, kuti adakhala pamodzi ndi Yesu.

14. Ndipotu pakuona munthu wociritsidwayoalikuimirira pamodzi nao, analibe kanthu kakunena kotsutsa.

15. Koma pamene anawalamulira iwo acoke m'bwalo la akulu, ananena wina ndi mnzace,

16. kuti, Tidzawacitira ciani anthu awa? pakutitu caoneka kwa onse akukhala m'Yerusalemu kuti cizindikilo cozindikirika cacitidwa ndi iwo, ndipo sitingathe kukana.

17. Komatu tiwaopse asalankhulenso m'dzina ili kwa munthu ali yense, kuti cisabukenso kwa anthu.

18. Ndipo anawaitana, nawalamulira kuti asanene konse kapena kuphunzitsa m'dzina la Yesu.

19. Koma Petro ndi Yohane anayankha nati kwa iwo, Weruzani, ngati nkwabwino pamaso pa Mulungu kumvera inu koposa Mulungu;

20. pakuti sitingatheife kuleka kulankhula zimene tinaziona ndi kuzimva.

21. Koma m'mene anawaopsanso anawamasula, osapeza kanthu kakuwalanga, cifukwa ca anthu; pakuti onse analemekeza Mulungu cifukwa ca comwe cidacitika.

22. Pakuti anali wa zaka zace zoposa makumi anai munthuyo, amene cizindikilo ici cakumciritsa cidacitidwa kwa iye.

23. Ndipo m'mene anamasulidwa, anadza kwa anzao a iwo okha, nawauza ziri zonse oweruza ndi akulu adanena nao.

24. Ndipo m'mene adamva, anakweza mau kwa Mulungu ndi mtima umodzi, nati, Mfumu, Inu ndinu wolenga thambo la kumwamba ndi dziko, ndi nyanja, ndi zonse ziri m'menemo;

25. amene mwa Mzimu Woyera, pakamwa pa kholo lathu Davine mtumiki wanu, mudati,Amitundu anasokosera cifukwaciani?Nalingirira zopanda pace anthu?

26. Anadzindandalitsa mafumu a dziko,Ndipo oweruza anasonkhanidwa pamodzi,Kutsutsana ndi Ambuye, ndi Kristu wace.

27. Pakuti zoonadi anasonkhanidwa m'mudzi muno Herode, ndi Pontiyo Pilato yemwe pamodzi ndi amitundu ndi anthu a Israyeli kumcitira coipa Mwana wanu wopatulika Yesu amene munamdzoza;

28. kuti acite ziri zonse dzanja lanu ndi uphungu wanu zidaweruziratu zicitike.

29. Ndipo tsopano Ambuye, penyani mau ao akuopsa, ndipo patsani kwa akapolo anu alankhule mau anu ndi kulimbika mtima konse,

30. m'mene mutambasula dzanja lanu kukaciritsa; ndi kuti zizindikilo ndi zozizwa zicitidwe mwa dzina la Mwana wanu wopatulika Yesu.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 4