Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 19:5-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Pamene anamva ici, anabatizidwa m'dzina la Ambuye Yesu.

6. Ndipo pamene Paulo anaika manja ace pa iwo, Mzimu Woyera anadza pa iwo; ndipo analankhula ndi malilime, nanenera.

7. Onsewo anali ngati amuna khumi ndi awiri.

8. Ndipo iye analowa m'sunagoge, nanena molimba mtima, miyezi itatu, natsutsana ndi kukopa kunena za Ufumu wa Mulungu.

9. Koma pamene ena anaumitsa mtima ndi kusamvera, nanenera zoipa Njirayo pamaso pa anthu, anawacokera, napatutsa akuphunzira, nafotokozera masiku onse m'sukulu ya Turano.

10. Ndipo anacita comweco zaka ziwiri; kotero kuti onseakukhala m'Asiya anamva mau a Ambuye, Ayuda ndi Ahelene.

11. Ndipo Mulungu anacita zamphamvu za pa zokha ndi manja a Paulo;

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 19