Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 19:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo panali, pamene Apolo anali ku Korinto, Paulo anapita pa maiko a pamtunda, nafika ku Efeso, napeza akuphunzira ena;

2. ndipo anati kwa iwo, Kodi munalandira Mzimu Woyera pamene munakhulupira? Ndipo anati, lai, sitinamva konsekuti Mzimu Woyera waperekedwa.

3. Ndipo anati, Nanga mwabatizidwa m'ciani? Ndipo anai, Mu ubatizo wa Yohane.

4. Ndipo anati Paulo, Yohane anabatiza ndi ubatizo wa kutembenuka mtima, nati kwa anthu, kuti amkhulupirire iye amene adzadza pambuyo pace, ndiye Yesu.

5. Pamene anamva ici, anabatizidwa m'dzina la Ambuye Yesu.

6. Ndipo pamene Paulo anaika manja ace pa iwo, Mzimu Woyera anadza pa iwo; ndipo analankhula ndi malilime, nanenera.

7. Onsewo anali ngati amuna khumi ndi awiri.

8. Ndipo iye analowa m'sunagoge, nanena molimba mtima, miyezi itatu, natsutsana ndi kukopa kunena za Ufumu wa Mulungu.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 19