Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 12:4-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo m'mene adamgwira, anamuika m'ndende, nampereka kwa magulu anai a alonda, lonse anai anai, amdikire iye; ndipo anafuna kumturutsa kudza naye kwa anthu atapita Paskha.

5. Pamenepo ndipo Petro anasungika m'ndende; koma Eklesia anampempherera iye kwa Mulungu kosalekeza.

6. Ndipo pamene Herode anati amturutse, usiku womwewo Petro analikugona pakati pa asilikari awiri, womangidwa ndi maunyolo awiri; ndipo alonda akukhalapakhomoanadikira ndende.

7. Ndipo taonani, mngelo wa Ambuye anaimirirapo, ndipo kuunika kunawala mokhalamo iye; ndipo anakhoma Petro m'nthiti, namuutsa iye, nanena, Tauka msanga, Ndipo maunyolo anagwa kucoka m'manja mwace.

8. Ndipo mngelo anati kwa iye, Dzimangire m'cuuno, numange nsapato zako. Nacita cotero. Ndipo ananena naye, Pfunda cobvala cako, nunelitsate ine.

9. Ndipo anaturuka, namtsata; ndipo sanadziwa kuti ncoona cocitidwa ndi mngelo, koma anayesa kuti alikuona masomphenya.

10. Ndipo m'mene adapitirira podikira poyamba ndi paciwiri, anadza ku citseko cacitsulo cakuyang'ana kumudzi; cimene cidawatsegukira cokha; ndipo anaturuka, napitirira khwalala limodzi; ndipo pomwepo mngelo anamcokera.

11. Ndipo Petro atatsitsimuka, anati, Tsopano ndidziwa zoona, kuti Ambuye anatuma mngelo wace nandilanditsa ine m'dzanja la Herode, ndi ku cilingiriro conse ca anthu a Israyeli.

12. Ndipo m'mene adalingirirapo, anadza ku nyumba ya Marlys amace wa Yohane wonenedwanso Marko; pamenepo ambiri adasonkhana pamodzi, ndipo analikupemphera,

13. Ndipo m'mene anagogoda pa citseko ca pakhomo, linadza kudzabvomera buthu, dzina lace Roda.

14. Ndipo pozindikira mau ace a Petro, cifukwa ca kukondwera sanatsegula pakhomo, koma anathamanga nalowanso, nawauza kuti Petro alikuima pakhomo.

15. Koma anati kwa iye, Wamisala iwe. Ndipo analimbika ndi kunena kuti nkutero. Ndipo ananena, Ndiye mngelo wace.

16. Koma Petro anakhala cigogodere; ndipo m'mene adamtsegulira, anamuona iye, nadabwa.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 12