Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 11:14-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. amene adzalankhula nawe mau, amene udzapulumutsidwa nao iwe ndi apabanja ako onse.

15. Ndipo m'mene ndinayamba kulankhula, Mzimu Woyera anawagwera, monga anatero ndi ife poyamba paja.

16. Ndipo ndinakumbuka mau a Ambuye, kuti ananena, Yohanetu anabatiza ndi madzi; koma inu mudzabatizidwa ndi Mzimu Woyera.

17. Ngati tsono Mulungu anawapatsa iwo mphatso yomweyi yonga ya kwa ife, pamene tinakhulupirira Ambuye Yesu Kristu, ndine yani kuti ndingathe kuletsa Mulungu?

18. Ndipo pamene anamva izi, anakhala du, nalemekeza Mulungu, ndi kunena, a Potero Mulungu anapatsa kwa amitundunso kutembenukira mtima kumoyo.

19. Pamenepo iwotu, akubalalika cifukwa ca cisautsoco cidadza pa Stefano, anafikira ku Foinike, ndi Kupro, ndi Antiokeya, osalankhula mau kwa wina yense koma kwa Ayuda okha.

20. Koma panali ena mwa iwo, amuna a ku Kupro, ndi Kurene, amenewo, m'mene adafika ku Antiokeya, analankhula ndi Ahelene, ndi kulalikira Uthenga Wabwino wa Ambuye Yesu.

21. Ndipo dzanja la Ambuye linali nao; ndi unyinji wakukhulupira unatembenukira kwa Ambuye.

22. Ndipo mbiri yao inamveka m'makutu a Mpingo wakukhala m'Yerusalemu; ndipo anatuma Bamaba apite kufikira ku Antiokeya;

23. ameneyo, m'mene anafika, naona cisomo ca Mulungu, anakondwa; ndipo anawandandaulira onse, kuti atsimikize mtima kukhalabe ndi Ambuye;

24. cifukwa anali munthu wabwino, ndi wodzala ndi Mzimu Woyera ndi cikhulupiriro: ndipo khamu lalikuru lidaonjezeka kwa Ambuye.

25. Ndipo anaturuka kunka ku Tariso kufunafuna Saulo;

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 11