Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 9:13-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Koma anati kwa iwo, Muwapatse kudya ndinu. Koma anati, Ife tiribe mikate, koma isanu yokha, ndi nsomba ziwiri zokha; kapena timuke ife kukagulira anthu awa onse zakudya.

14. Pakuti anali amuna ngati zikwi zisanu. Koma iye anati kwa ophunzira ace, Khalitsani iwo pansi magulu magulu, ngati makumi asanu asanu.

15. Ndipo anatero, nawakhalitsa pansi onsewo.

16. Ndipo iye, m'mene anatenga mikate isanu ija ndi nsomba ziwiri anayang'ana kumwamba, nazidalitsa, nanyema, napatsa ophunzira apereke kwa anthuwo.

17. Ndipo anadya, nakhuta onsewo; natola makombo, mitanga khumi ndi iwiri.

18. Ndipo kunali, pamene iye analikupemphera padera, ophunzira anali naye; ndipo anawafunsa iwo, kuti, Makamuwo a anthu anena kuti Ine ndine yani?

19. Ndipo anayankha nati, Yohane Mbatizi; koma ena, Eliya; ndi ena, kuti anauka mmodzi wa aneneri akale.

20. Ndipo anati kwa iwo, Koma inu munena kuti Ine ndine yani? Ndipo anayankha Petro, nati, Kristu wa Mulungu.

21. Ndipo iye anawauzitsa iwo, nalamulira kuti asanene ici kwa munthu ali yense;

22. nati, Kuyenera kuti Mwana wa munthu amve zowawa zambiri, ndi kukanidwa ndi akuru, ndi ansembe akuru, ndi alembi, ndi kuphedwa, ndi kuuka tsiku lacitatu.

Werengani mutu wathunthu Luka 9