Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 4:25-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Koma zoonadi ndinena kwa inu, kuti, Munali akazi amasiye ambiri m'lsrayeli masiku ace a Eliya, pamene kunatsekedwa kumwamba zaka zitatu ndi miyezi isanu ndi umodzi, pamene panakhala njala yaikuru pa dziko lonselo;

26. ndipo Eliya sanatumidwa kwa mmodzi wa iwo, koma ku Sarepta wa ku Sidoniya, kwa mkazi wamasiye.

27. Ndipo munali akhate ambiri m'Israyeli masiku a Elisa mneneri; ndipo palibe mmodzi wa iwo anakonzedwa, koma Namani yekha wa ku Suriya.

28. Ndipo onse a m'sunagogemo anadzala ndi mkwiyo pakumva izi;

29. nanyamuka na mturutsira Iye kunja kwa mudziwo, nanka naye pamutu pa phiri pamene panamangidwa mudzi wao, kuti akamponye iye pansi.

30. Koma iye anapyola pakati pao, nacokapo.

31. Ndipo iye anatsika nadza ku Kapernao, ndiwo mudzi wa ku Galileya, Ndipo analikuwaphunzitsa iwo pa Sabata; ndipo anadabwa ndi ciphunzitso cace;

32. cifukwa mau ace anali ndi ulamuliro.

33. Ndipo munali m'sunagoge munthu, wokhala naco ciwanda conyansa; napfuula ndi mau olimba, kuti,

34. Ha! tiri ndi ciani ndi Inu, Yesu wa ku N azarete? kodi munadza kutiononga ife? ndikudziwani Inu muli yani, ndinu Woyera wace wa Mulungu.

35. Ndipo Yesu anamdzudzula iye, nanena, Tonthola, nuturuke mwa iye. Ndipo ciwandaco m'mene cinamgwetsa iye pakati, cinaturuka mwa iye cosampweteka konse.

Werengani mutu wathunthu Luka 4