Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 3:5-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Cigwa ciri conse cidzadzazidwa,Ndipo phiri liri lonse ndi mtunda uti wonse zidzacepsedwa;Ndipo zokhota zidzakhala zolungama,Ndipo njira za zigoloondo zidzakhala zosalala;

6. Ndipo anthu onse adzaona cipulumutso ca Mulungu.

7. Cifukwa cace iye ananena kwa makamuwo a anthu amene anaturukira kukabatizidwa ndi iye, Obadwa a njoka inu, anakulangizani inu ndani kuthawa mkwiyo ulinkudza?

8. Cifukwa cace balani zipatso zakuyenera kulapa mtima, ndipo musayambe kunena mwa inu nokha, Atate wathu tiri naye ndiye Abrahamu: pakuti ndinena kwa inu, kuti ali ndi mphamvu Mulungu, mwa miyala iyi, kuukitsira Abrahamu ana.

9. Ndiponso tsopano lino nkhwangwa yaikidwa pa mizu ya mitengo; cotero mtengo uli wonse wosabala cipatso cabwino udulidwa, nuponyedwa pamoto.

10. Ndipo anthu a makamu anamfunsa iye, nanena, Ndipo tsono tizicita ciani?

11. Koma iye anayankha nanena kwa iwo, Iye amene ali nao malaya awiri apatse kwa iye amene alibe; ndi iye amene ali nazo zakudya acite comweco.

12. Ndipo amisonkho omwe anadza kudzabatizidwa, nati kwa iye, Mphunzitsi, ife tizicita ciani?

13. Koma iye anati kwa iwo, Musakapambe kanthu konse kakuposa cimene anakulamulirani.

14. Ndipo asilikari omwe anamfunsa iye, nati, Nanga ife tizicita ciani? Ndipo iye anati kwa iwo, Musaopse, musanamize munthu ali yense; khalani okhuta ndi kulipira kwanu.

15. Ndipo pamene anthu anali kuyembekezera, ndipo onse anaganizaganiza m'mitima yao za Yohane, ngati kapena iye ali Kristu;

16. Yohane anayankha, nanena kwa onse, Inetu ndikubatizani inu ndi madzi; koma wakundiposa ine mphamvu alinkudza, amene sindiyenera kumasula lamba la nsapato zace; Iyeyu adzakubatizani inu ndi Mzimu Woyera ndi moto:

17. amene couluzira cace ciri m'dzanja lace, kuti ayeretse padwale pace, ndi kusonkhanitsa tirigu m'ciruli cace; koma mankhusu adzatentha m'moto wosazima.

18. Coteretu iye anauza anthu Uthenga Wabwino ndi kuwadandaulira zinthu zina zambiri.

19. Koma Herode mfumu ija, m'mene Yohane anamdzudzula cifukwa ca Herodiya, mkazi wa mbale wace, ndi ca zinthu zonse zoina Herode anazicita,

20. anaonjeza pa zonsezi icinso, kuti anatsekera Yohane m'nyumba yandende.

21. Ndipo panali pamene anthu onse anabatizidwa, ndipo Yesu anabatizidwa, nalikupemphera, kuti panatseguka pathambo,

Werengani mutu wathunthu Luka 3