Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 16:19-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ndipo panali munthu mwini cuma amabvala cibakuwa ndi nsaru yabafuta, nasekera, nadyerera masiku onse;

20. ndipo wopemphapempha wina, dzina lace Lazaro, adaikidwa pakhomo pace wodzala ndi zironda,

21. ndipo anafuna kukhuta ndi zakugwa pa gome la mwini cumayo; komatu agarunso anadza nanyambita zirondazace.

22. Ndipo kunali kuti wopemphayo adafa, ndi kuti anatengedwa iye ndi angelo kunka ku cifuwa ca Abrahamu; ndipo mwini cumayo adafanso, naikidwa m'manda.

23. Ndipo m'Hade anakweza maso ace, pokhala nao mazunzo, naona Abrahamu patali, ndi Lazaro m'cifuwa mwace.

24. Ndipo anakweza mau nati, Atate Abrahamu, mundicitire cifundo, mutome Lazaro, kuti abviike nsonga ya cala cace m'madzi, naziziritse lilime langa; pakuti ndizunzidwadi m'lawi ili la moto.

25. Koma Abrahamu anati, Mwana, kumbukila kuti unalandira zokoma zako pakukhala m'moyo iwe, momwemonso Lazaro zoipa; ndipo tsopano iye asangalatsidwa pano, koma iwe uzunzidwadi.

Werengani mutu wathunthu Luka 16