Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 13:12-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo Yesu m'mene anamuona, anamuitana, nanena naye, Mkaziwe, wamasulidwa kudwala kwako.

13. Ndipo anaika manja ace pa iye; ndipo pomwepo anaongoledwa, nalemekeza Mulungu.

14. Ndipo mkuru wa sunagoge anabvutika mtima, cifukwa Yesu anaciritsa tsiku la Sabata, nayankha, nanena kwa khamulo, Alipo masiku asanu ndi limodzi, m'menemo anthu ayenera kugwira nchito, cifukwa cace idzani kudzaciritsldwa momwemo, koma tsiku la Sabata ai.

15. Koma Ambuye anamyankha iye, nati, Onyenga inu, kodi munthu ali yense wa inu samaimasula ng'ombe yace, kapena buru wace kucodyeramo, tsiku la Sabata, kupita nayo kukaimwetsa madzi?

16. Ndipo mkazi uyu, ndiye mwana wa Abrahamu, amene Satana anammanga, onani, zaka khumi ndi zisanu ndi zitatu, nanga si kuyenera kodi, kuti amasulidwe nsinga yace imeneyi tsiku la Sabata?

17. Ndipo pamene Iye anatero, onse aja akutsutsana naye ananyazitsidwa; ndipo anthu onse a m'khamu anakondwera ndi zinthu zonse za ulemererozo zinacitidwa ndi iye.

18. Pamenepo ananena, Ufumu wa Mulungu ufanana ndi ciani? ndipo ndidzaufanizira ndi ciani?

19. Ufanana ndi kambeu kampiru, kamene munthu anatenga, nakaponya m'munda wace wace, ndipo kanamera, kanakula mtengo; ndi mbalame za m'mlengalenga zinabindikira mu nthambi zace.

20. Ndiponso anati, Ndidzafanizira Ufumu wa Mulungu ndi ciani?

21. Ufanana ndi cotupitsa mikate, cimene mkazianatenga, nacibisa mu miyeso itatu ya ufa, kufikira unatupa wonsewo,

22. Ndipo Iye anapita pakati pa mizinda ndi midzi, naphunzitsa, nayenda ulendo kunkabe ku Yerusalemu.

23. Ndipo munthu anati kwa iye, Ambuye, akupulumutsidwandiwo owerengeka kodi? Koma iye anati kwa iwo,

24. Yesetsani kulowa pa khomo lopapatiza; cifukwa anthu ambiri, ndikuuzani, adzafunafuna kulowamo, koma sadzakhoza.

Werengani mutu wathunthu Luka 13