Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 11:32-42 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

32. Amuna a ku Nineve adzaimirira pa mlandu wotsiriza pamodzi ndi anthu a mbadwo uno, nadzawatsutsa; pakuti iwo analapa pa kulalikira kwa Y ona; ndipo onani, wakuposa Y ona ali pano.

33. Palibe munthu, atayatsa nyali, aiika m'cipinda capansi, kapena pansi pa muyeso, koma pa coikapo cace, kuti iwo akulowamo aone kuunika.

34. Nyali ya thupi ndiyo diso lako; pamene pali ponse diso lako liri langwiro thupi lako lonse liunikidwanso monsemo; koma likakhala loipa, thupi lako lomwe liri la mdima wokha wokha.

35. Potero yang'anira kuunika kuli mwa iwe kungakhale mdima.

36. Pamenepo, ngati thupi lako lonse liunikidwa losakhala nalo dera lace lamdima, lidzakhala lounikidwa monsemo, ngati pamene nyali ndi kuwala kwace ikuunikira iwe.

37. Ndipo pakulankhula iye, anamuitana Mfarisi kuti adye naye; ndipo analowa naseama kudya.

38. Ndipo anazizwa Mfarisiyo, pakuona kuti anayamba cakudya asanasambe.

39. Koma Ambuye anati kwa iye, Tsopano inu Afarisi muyeretsa kunja kwace kwa cikho ndi mbale, koma m'kati mwanu mudzala zolanda ndi zoipa.

40. Opusa inu, kodi iye wopanga kunja kwace sanapanganso m'kati mwace?

41. koma patsani mphatso yacifundo za m'katimo; ndipo onani, zonse ziri zoyera kwa inu.

42. Koma tsoka inu, Afarisi! cifukwa mupereka limodzi la magawo khumi la timbeu tonunkhira, ndi timbeu tokometsa cakudya ndi ndiwo zonse, ndipo mumaleka ciweruziro ndi cikondi ca Mulungu; mwenzi mutacita izi, ndi kusasiya zinazo.

Werengani mutu wathunthu Luka 11