Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 11:29-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Ndipo pakusonkhana pamodzi makamu a anthu, anayamba kunena, Mbadwo uno ndi mbadwo woipa; ufuna cizindikilo, ndipo cizindikilo sicidzapatsidwa kwa uwu koma cizindikilo ca Yona.

30. Pakuti monga ngati Yona anali cizindikilo kwa Anineve, cotero adzakhalanso Mwana wa munthu kwa mbadwo uno.

31. Mfumu yaikazi ya kumwera idzaimirira pa mlandu wotsiriza pamodzi ndi amuna a mbadwo uno, nadzawatsutsa; pakuti anadza ku'cokera ku malekezero a dziko kudzamva nzeru za Solomo; ndipo onani, woposa Solomo ali pano.

32. Amuna a ku Nineve adzaimirira pa mlandu wotsiriza pamodzi ndi anthu a mbadwo uno, nadzawatsutsa; pakuti iwo analapa pa kulalikira kwa Y ona; ndipo onani, wakuposa Y ona ali pano.

33. Palibe munthu, atayatsa nyali, aiika m'cipinda capansi, kapena pansi pa muyeso, koma pa coikapo cace, kuti iwo akulowamo aone kuunika.

34. Nyali ya thupi ndiyo diso lako; pamene pali ponse diso lako liri langwiro thupi lako lonse liunikidwanso monsemo; koma likakhala loipa, thupi lako lomwe liri la mdima wokha wokha.

35. Potero yang'anira kuunika kuli mwa iwe kungakhale mdima.

36. Pamenepo, ngati thupi lako lonse liunikidwa losakhala nalo dera lace lamdima, lidzakhala lounikidwa monsemo, ngati pamene nyali ndi kuwala kwace ikuunikira iwe.

Werengani mutu wathunthu Luka 11