Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 9:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo mngelo wacisanu anaomba, ndipo ndinaona nyenyezi yocokera kumwamba idagwa padziko; ndipo anampatsa iye cifunguliro ca dzenje la phompho.

2. Ndipo anatsegula pa dzenje la phompho; ndipo unakwera utsi woturuka m'dzenjemo, ngati utsi wa ng'anjo yaikuru; ndipo dzuwa ndi thambo zinada, cifukwa ca utsiwo wa kudzenje,

3. Ndipo m'utsimo mudaturuka dzombe padziko, ndipo analipatsa ilo mphamvu monga zinkhanira za dziko ziri ndi mphamvu.

4. Ndipo ananena kwa ilo kuti lisaipse udzu wa padziko, kapena cabiriwiri ciri conse, kapena mtengo uli wonse, koma anthu amene alibe cizindikilo ca Mulungu pamphumi pao ndiwo.

5. Ndipo anapatsa ilo mphamvu si kuti likawaphe, komatu kuti likawazunze miyezi isanu; ndipo mazunzidwe ao anali ngati mazunzidwe a cinkhanira, pamene ciluma munthu.

6. Ndipo m'masiku ajawo, anthu adzafunafuna imfa osaipeza konse; ndipo adzakhumba kumwalira, koma imfa idzawathawa.

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 9