Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 5:7-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo anadza, nalitenga ku dzanja lamanja la Iye wakukhala pa mpando wacifumu.

8. Ndipo pamene adatenga bukulo, zamoyo zinai ndi akulu makumi awiri mphambu anai zinagwa pansi pamaso pa Mwanawankhosa, zonse ziri nao azeze, ndi mbale zagolidi zodzala ndi zofukiza, ndizo mapemphero a oyera mtima.

9. Ndipo ayimba nyimbo yatsopano, ndi kunena, Muyenera kulandira bukulo, ndi kumasula zizindikilo zace; cifukwa mwaphedwa, ndipo mwagulira Mulungu ndi mwazi wanu anthu a mafuko onse, ndi manenedwe onse, ndi mitundu yonse,

10. ndipo mudawayesa iwo ufumu ndi ansembe kwa Mulungu wathu; ndipo acita ufumu padziko.

11. Ndipo ndinaona, ndipo ndinamva mau a angelo ambiri pozinga mpando wacifumu, ndi zamoyo ndi akulu; ndipo mawerengedwe ao anali zikwi khumi kucurukitsa zikwi khumi ndi zikwiza zikwi;

12. akunena ndi mau akulu, Ayenera Mwanawankhosa, wophedwayo, kulandira cilimbiko, ndi cuma, ndi nzeru, ndi mphamvu, ndi ulemu, ndi ulemerero, ndi ciyamiko.

13. Ndipo colengedwa ciri conse ciri m'mwamba, ndi padziko, ndi pansi pa dziko, ndi m'nyanja, ndi zonse ziri momwemo, ndinazimva zirikunena, Kwa iye wakukhala pa mpando wacifumu, ndi kwa Mwanawankhosa zikhale ciyamiko, ndi ulemu, ndi ulemerero, ndi ufumu, kufikira nthawi za nthawi.

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 5