Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 22:1-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo anandionetsa mtsinje wa madzi a moyo, wonyezimira ngati krustalo, oturuka ku mpando wacifumu wa Mulungu ndi wa Mwanawarikhosa.

2. Pakati pa khwalala lace, ndi tsidya ili la mtsinje, ndi tsidya lace lija panali mtengo wa moyo wakubala zipatso khumi ndi ziwiri, ndi kupatsa zipatso zace mwezi ndi mwezi; ndipo masamba a mtengo ndiwo akuciritsa nao amitundu.

3. Ndipo sipadzakhalanso temberero liri lonse; ndipo mpando wacifumu wa Mulungu ndi wa Mwanawankhosa udzakhala momwemo; ndipo akapolo ace adzamtumikira iye,

4. nadzaona nkhope yace; ndipo dzina lace lidzakhala pamphumipao.

5. Ndipo sikudzakhalanso usiku; ndipo sasowa kuunika kwa nyali, ndi kuunika kwa dzuwa; cifukwa Ambuye Mulungu adzawaunikira; ndipo adzacita ufumu ku nthawi za nthawi.

6. Ndipo anati kwa ine, Mau awa ali okhulupirika ndi oona; ndipo Ambuye, Mulungu wa mizimu ya aneneri, anatuma mngelo wace kukaonetsera akapolo ace zimene ziyenera kucitika msanga.

7. Ndipo taonani, ndidza msanga. Wodala iye amene asunga mau a cinenero ca buku ili.

8. Ndipo ine Yohane ndine wakumva ndi wakupenya izi. Ndipo pamene ndinamva ndi kupenya, ndinagwa pansi kulambira pa mapazi a mngelo wakundionetsa izo.

9. Ndipo ananena kwa ine, Tapenya, usacite; ndine kapolo mnzako, ndi mnzao wa abale ako aneneri, ndi wa iwo akusunga mau a buku ili; lambira Mulungu.

10. Ndipo ananena ndi ine, Usasindikiza cizindikilo mau a cinenero ca buku ili; pakuti nthawi yayandikira.

11. Iye wakukhala wosalungama acitebe zosalungama; ndi munthu wonyansa akhalebe wonyansa; ndi iye wakukhala wolungama acitebe colungama; ndi iye amene ali woyera akhalebe woyeretsedwa.

12. Taonani, ndidza msanga; ndipo mphotho yanga ndiri nayo yakupatsa yense monga mwa nchito yace.

13. Ine ndine Alefa ndi Omega, woyamba ndi wotsiriza, ciyambi ndi citsiriziro.

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 22