Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 18:15-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Otsatsa izi, olemezedwa nao, adzaima patali cifukwa ca kuopa cizunzo cace, nadzalira, ndi kucita cifundo;

16. nadzanena, Tsoka, tsoka, mudzi waukuru wobvala bafuta ndi cibakuwa, ndi mlangali, wodzikometsera ndi golidi, ndi mwala wa mtengo wace, ndi ngale!

17. Pakuti m'ora limodzi casanduka bwinja cuma cacikuru cotere. Ndipo watsigiro ali yense, ndi yense wakupita panyanja pakuti pakuti, ndi amarinyero, ndi onse amene amacita kunyanja, anaima patali,

18. napfuula poona utsi wa kutentha kwace, nanena, Mudzi uti ufanana ndi mudzi waukuruwo?

19. Ndipo anathira pfumbi pamitu pao, napfuula, ndi kulira, ndi kucita maliro, nanena, Tsoka, tsoka, mudzi waukuruwo, umene analemerezedwa nao onse akukhala nazo zombo panyanja, cifukwa ca kulemera kwace, pakuti m'ora limodzi unasanduka bwinja.

20. Kondwera pa iye, m'mwamba iwe, ndi oyera mtima, ndi atumwi, ndi aneneri inu; cifukwa Mulungu anauweruzira kuweruzidwa kwanu.

21. Ndipo mngelo wolimba ananyamula mwala, ngati mphero yaikuru, naiponya m'nyanja, nanena, Cotero Babulo, mudzi waukuru, udzapasulidwa kolimba, ndipo sudzapezedwanso konse.

22. Ndipo mau a anthu oyimba zeze, ndi a oyimba, ndi a oliza zitoliro, ndi a oomba malipenga sadzamvekanso konse mwa iwe; ndipo nunisiri ali yense wa macitidwe ali onse sadzapezedwanso konse mwa iwe; ndi mau a mphero sadzamvekanso konse mwa iwe;

23. 1 ndi kuunika kwa nyali sikudzaunikiranso konse mwa iwe; ndi mau a mkwati ndi a mkwatibwi sadzamvekanso konse mwa iwe; pakuti otsatsa malonda anu anali omveka a m'dziko; pakuti 2 ndi nyanga yako mitunduyonse inasokeretsedwa.

24. Ndipo 3 momwemo munapezedwa mwazi wa aneneri ndi oyera mtima, ndi onse amene anaphedwa padziko.

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 18