Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 17:3-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo ananditenga kumka nane kucipululu, mu Mzimu; ndipo ndinaona mkazi alinkukhala pacirombo cofiiritsa, codzala ndi maina a mwano, cakukhala nayo mitu isanu ndi iwiri ndi nyanga khumi.

4. Ndipo mkazi anabvala cibakuwa, ndi mlangali, nakometsedwa ndi golidi, ndi miyala ya mtengo wace, ndi ngale; nakhala naco m'dzanja lace cikho cagolidi codzala ndi zonyansitsa, ndi zodetsa za cigololo cace,

5. ndipo pamphumi pace padalembedwa dzina, CINSINSI, BABULO WAUKURU AMAI WA ACIGOLOLO NDI WA ZONY ANSITSA ZA DZIKO.

6. Ndipo ndinaona mkazi woledzera ndi mwazi wa oyera mtima, ndi mwazi wa mboni za Yesu; ndipo ndinazizwa pakumuona iye ndi kuzizwa kwakukuru.

7. Ndipo mngelo anati kwa ine, Uzizwa cifukwa ninji? ine ndidzakuuza iwe cinsinsi ca mkazi, ndi ca cirombo cakumbereka iye, cokhala nayo mitu isanu ndi iwiri ndi nyanga khumi.

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 17