Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ahebri 8:1-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Koma mutu wafzi tanenazi ndi uwu: Tiri naye Mkuruwansembe wotere, amene anakhala pa dzanja lamanja la mpando wacifumu wa Ukulu m'Kumwamba,

2. Mtumiki wa malo opatulika, ndi wa cihema coona, cimene Ambuye anacimanga, si munthu ai.

3. Pakuti mkulu wa ansembe ali yense aikidwa kupereka mitulo, ndiponso nsembe; potero nkufunika kuti ameneyo akhale nako kanthunso kakupereka,

4. Ndipo iye akadakhala padziko, sakadakhala konse wansembe, popeza pali iwo akupereka mitulo monga mwa lamulo;

5. amene atumikira cifaniziro ndi mthunzi wa zakumwambazo monga Mose acenjezedwa m'mene anafuna kupanga cihema: pakuti, Cenjera, ati, ucite zonse monga mwa citsanzoco caonetsedwa kwa iwe m'phiri.

6. Koma tsopano iye walandira citumikiro comveka coposa, umonso ali Nkhoswe ya pangano labwino loposa, limene likhazikika pa malonjezano oposa.

7. Pakuti loyamba lija likadakhala lopanda cirema sakadafuna malo a laciwirilo.

8. Pakuti powachulira iwo cifukwa, anena,Taonani, akudza masiku, anena Ambuye,Ndipo ndidzapangana pangano latsopano ndi nyumba ya Israyeli, ndi nyumba ya Yuda,

9. Losati longa pangano ndinalicita ndi makolo ao,Tsikuli ndinawagwira kudzanja iwo kuwatsogolera aturuke m'dziko la Aigupto;Kuti iwo sanakhalabe m'pangano langa,Ndipo loe sindinawasamalira iwo, anena Ambuye,

Werengani mutu wathunthu Ahebri 8