Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Agalatiya 2:15-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ife ndife Ayuda pacibadwidwe, ndipo sitiri ocimwa a kwaamitundu;

16. koma podziwa kuti munthu sayesedwa wolungama pa: nchito ya lamulo, koma mwa cikhulupiriro ca Yesu Kristu, ifedi tinakhulupirira kwa Yesu Kristu, kuti tikayesedwe olungama ndicikhulupiriro ca Kristu, ndipo si ndi nchito za lamulo; pakuti palibe munthu adzayesedwa wolungama ndi nchito za lamulo.

17. Koma ngati ife, pofuna kuyesedwa olungama mwa Kristu, tipezedwanso tiri ocimwa tokha, kodi Kristu ali mtumikiwa ucimo cifukwa cace? Msatero ai.

18. Pakuti ngati izi zomwezi ndazigumula ndizimanganso, ndidzitsimikizira ndekha ndirt wolakwa.

19. Pakuti ine mwa lamulo ndafa ku lamulo, kuti ndikhale ndi moyo kwa Mulungu.

20. Ndinapacikidwa ndi Kristu; koma ndiri ndi mayo; wosatinso ine ai, koma Kristu ali ndi moyo mwa ine; koma moyo umene ndiri nao: tsopano m'thupi, ndiri nao m'cikhulupiriro ca Mwana wa Mulungu, amene anandikonda, nadzipereka yekha cifukwa ca ine.

21. Sindieiyesa copanda pace cisomo ca Mulungu; pakuti ngati cilungamo ciri mwa Lamulo, Kristu adafa cabe.

Werengani mutu wathunthu Agalatiya 2