Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoweli 2:21-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Usaopa, dziko iwe; kondwera, nusekerere; pakuti Yehova wacita zazikuru.

22. Musamaopa, nyama za kuthengo inu; pakuti m'cipululu muphukanso msipu; pakuti mitengo ibala zipatso zao; mikuyu ndi mipesa ipatsa mphamvu zao.

23. Mukondwere tsono, inu ana a Ziyoni, nimusekerere m'Yehova Mulungu wanu; pakuti adzayamba kukupatsani mvula yamyundo, monga mwa cilungamo cace; nakubvumbitsirani mvula, mvula yamyundo ndi yamasika mwezi woyamba.

24. Ndipo madwale adzakhala ndi tirigu, ndi vinyo, ndi mafuta; zidzasefuka m'zosungiramo zao.

25. Ndipo ndidzakubwezerani zaka zidazidya dzombe, ndi cirimamine, ndi anoni, ndi cimbalanga, gulu langa lalikuru la nkhondo, limene ndinalitumiza pakati pa inu.

26. Ndipo mudzadyaidya ndi kukhuta, nimudzalemekeza dzina la Yehova Mulungu wanu, amene anacita nanu modabwiza; ndi anthu anga sadzacita manyazi nthawi zonse.

27. Ndipo mudzadziwa kuti Ine ndiri pakati pa Israyeli, ndi kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, palibe wina; ndi anthu anga sadzacita manyazi nthawi zonse.

28. Ndipo kudzacitika m'tsogolo mwace, ndidzatsanulira mzimu wanga pa anthu onse, ndi ana anu amuna ndi akazi adzanenera, akulu akulu anu adzalota maloto, anyamata anu adzaona masomphenya;

29. ndi pa akapolo ndi adzakazi omwe ndidzatsanulira mzimu wanga masiku awo.

30. Ndipo ndidzaonetsa zodabwiza kuthambo ndi pa dziko lapansi, mwazi, ndi moto, ndi utsi tolo.

31. Dzuwa lidzasanduka mdima, ndi mwezi udzasanduka mwazi, lisanadze tsiku la Yehova lalikuru ndi loopsa.

32. Ndipo kudzacitika kuti ali yense adzaitana pa dzina la Yehova adzapulumutsidwa; pakuti m'phiri la Ziyoni ndi m'Yerusalemu mudzakhala cipulumutso, monga Yehova anatero, ndi mwa otsala amene Yehova adzawaitana.

Werengani mutu wathunthu Yoweli 2