Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 8:26-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Popeza Yoswa sanabweza dzanja lace limene anatambasula nalo nthungo, mpaka ataononga konse nzika zonse za ku Ai.

27. Koma ng'ombe ndi zofunkha za mudzi uwu Israyeli anadzifunkhira monga mwa mau a Yehova amene analamulira Yoswa.

28. Ndipo Yoswa anatentha Ai, nausandutsa muunda ku nthawi yonse, bwinja kufikira lero lino.

29. Ndipo mfumu ya ku Ai, anampacika pamtengo mpaka madzulo; koma polowa dzuwa Yoswa analamulira kuti atsitse mtembo wace pamtengo; ndipo anauponya polowera pa cipata ca mudzi; nauniikako mulu waukuru wamiyala, mpaka lero lino.

30. Pomwepo Yoswa anamangira Yehova Mulungu wa Israyeli guwa la nsembe m'phiri la Ebala,

31. monga Mose mtumiki wa Mulungu adalamulira ana a Israyeli, monga mulembedwa m'buku la cilamulo ca Mose, guwa la nsembe la miyala yosasema, yoti palibe munthu anakwezapo citsulo; ndipo anafukizirapo Yehova nsembe zopsereza, naphera nsembe zoyamika.

32. Ndipo analembapo pa miyalayi citsanzo ca cilamulo ca Mose, cimene analembera pamaso pa ana a Israyeli.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 8