Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 8:20-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Pamene amuna a ku Ai anaceuka, anapenya, ndipo taonani, utsi wa mudzi unakwera kumwamba; nasowa mphamvu iwo kuthawa cakuno kapena cauko; ndi anthu othawira kucipululu anatembenukira owapitikitsa.

21. Ndipo pakupenya Yoswa ndi Israyeli yense kuti olalirawo adagwira mudzi, ndi kuti utsi wa mudzi unakwera, anabwerera, nawapha amuna a ku Ai.

22. A kumudzinso anawaturukira; potero anakhala pakati pa Israyeli, ena mbali yina, ena mbali yina; ndipo anawakantha, mpaka sanatsala kapena kupulumuka wa iwo ndi mmodzi yense.

23. Koma mfumu ya ku Ai anamgwira wamoyo, nadza naye kwa Yoswa.

24. Ndipo kunali, atatha Israyeli kupha nzika zonse za ku Ai, kuthengo, kucipululu kumene anawapitikitsira, natha onse kugwa ndi lupanga lakuthwa mpaka adathedwa onse, Aisrayeli onse anabwerera ku Ai, naukantha ndi lupanga lakuthwa.

25. Ndipo onse amene adagwa tsiku lija, amuna ndi akazi, ndiwo zikwi khumi ndi ziwiri, anthu onse a ku Ai.

26. Popeza Yoswa sanabweza dzanja lace limene anatambasula nalo nthungo, mpaka ataononga konse nzika zonse za ku Ai.

27. Koma ng'ombe ndi zofunkha za mudzi uwu Israyeli anadzifunkhira monga mwa mau a Yehova amene analamulira Yoswa.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 8