Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 6:15-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndipo kunali, tsiku lacisanu ndi ciwiri analawira mamawa, mbandakuca, nazungulira mudzi mommuja kasanu ndi kawiri; koma tsiku lijalo anazungulira mudzi kasanu ndi kawiri.

16. Ndipo kunali, pa nthawi yacisanu ndi ciwiri, pamene ansembe analiza mphalasa, Yoswa anati kwa anthu, Pfuulani; pakuti Yehova wakupatsani mudziwo.

17. Koma mudziwo udzaperekedwa kwa Yehova ndi kuonongeka konse, uwu ndi zonse ziri m'mwemo; Rahabi yekha wadamayo adzakhala ndi moyo, iye ndi onse ali naye m'nyumba, cifukwa anabisa mithenga tinawatumawo.

18. Ndipo inu, musakhudze coperekedwaco, mungadziononge konse, potapa coperekedwaco; ndi kuononga konse cigono ca Israyeli ndi kucisautsa.

19. Koma siliva yense, ndi golidi yense, ndi zotengera za mkuwa ndi citsulo zikhala copatulikira Yehova; zilowe m'mosungira cuma ca Yehova.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 6