Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 5:12-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Koma m'mawa mwace mana analeka, atadya iwo tirigu wakhwimbi wa m'dziko; ndipo ana a Israyeli analibenso mana; koma anadya zipatso za dziko la Kanani caka comwe cija.

13. Ndipo kunali, pokhala Yoswa ku Yeriko, anakweza maso ace, napenya, ndipo taona, panaima muthu pandunji pace ndi lupanga lace losolola m'dzanja lace; namuka Yoswa kuli iye, nati iye, Ubvomerezana ndi ife kapena ndi aelani athu?

14. Nati, lai, koma ndadza ine, kazembe wa ankhondo a Yehova. Pamenepo Yoswa anagwa nkhope yace pansi, napembedza, nati kwa iye, Anenanji Ambuyanga kwa mtumiki wace?

15. Ndipo kazembe wa ankhondo a Yehova anati kwa Yoswa, Bvula nsapato yako pa phazi lako; pakuti malo upondapo mpopatulika. Nacita Yoswa comweco.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 5