Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 24:20-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Mukasiya Yehova, ndi kutumikira milungu yacilendo, adzatembenuka ndi kukucitirani coipa, ndi kukuthani, angakhale anakucitirani cokoma.

21. Ndipo anthu anati kwa Yoswa, Iaitu, koma tidzatumikira Yehova.

22. Ndipo Yoswa ananena ndi anthu, Inu mwadzicitira mboni inu nokha kuti mwadzisankhira Yehova kumtumikira iye. Ndipo anati, Ndife mboni.

23. Ndipo tsopano, cotsani milungu yacilendo iri pakati pa inu, ndi kulozetsa mitima yanu kwa Yehova, Mulungu wa Israyeli.

24. Ndipo anthu anati kwa Yoswa, Tidzamtumikira Yehova Mulungu wathu ndi kumvera mau ace.

25. Motero Yoswa anacita pangano ndi anthu tsiku lija, nawaikira lemba ndi ciweruzo m'Sekemu.

26. Ndipo Yoswa analembera mau awa m'buku la cilamulo ca Mulungu; natenga mwala waukuru, nauimitsa apo patsinde pa thundu wokhala pa malo opatulika a Yehova.

27. Ndipo Yoswa anati kwa anthu onse, Taonani, mwala uwu udzakhala mboni yotitsutsa; pakuti udamva mau onse a Yehova amene ananena kwa ife; ndipo udzakhala mboni yotsutsa inu, mungakanize Mulungu wanu.

28. Pamenepo Yoswa anauza anthu amuke, yense ku colowa cace.

29. Ndipo kunali, zitatha izi, Yoswa mwana wa Nuni mtumiki wa Yehova, adafa, wa zaka zana ndi khumi.

30. Ndipo anamuika m'malire a colowa cace m'Timinati-sera, ndiwo ku mapiri a Efraimu kumpoto kwa phiri la Gaasi.

31. Ndipo Israyeli anatumikira Yehova masiku onse a Yoswa, ndi masiku onse a akulu akulu otsala atafa Yoswa, amene anadziwa nchito yonse ya Yehova anaicitira Israyeli.

32. Ndipo mafupa a Yosefe amene ana a Israyeli anakwera nao kucokera ku Aigupto anawaika ku Sekemu, pa kadziko kamene adakagula Yakobo kwa ana a Hamori atate wa Sekemu ndi kuwapatsa ndalama zana; ndipo anakhala colowa ca ana a Yosefe.

33. Eleazarenso mwana wa Aroni anafa; ndipo anamuika pa phiri la Pinehasi mwana wace, limene adampatsa ku mapiri a Efraimu.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 24