Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 22:15-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. M'mene anafika kwa ana a Rubeni, ndi ana a Gadi, ndi pfuko la Manase logawika pakati, ku dziko la Gileadi, ananena nao ndi kuti,

16. Utero msonkhano wonse wa Yehova, Colakwa ici nciani mwalakwira naco Mulungu wa Israyeli, ndi kumtembenukira Yehova lero line kusamtsatanso, popeza munadzimangira guwa la nsembe kupikisana ndi Yehova lero lino?

17. Kodi mphulupulu ya ku Peori iticepera, imene sitinadziyeretsera mpaka lero lino, ungakhale mliri unadzera msonkhano wa Yehova,

18. kuti mubwerera lero line kusatsata Yehova? ndipo kudzakhala kuti popeza lero mupikisana ndi Yehova, mawa adzakwiyira msonkhano wonse wa Israyeli.

19. Koma mukayesa dziko La colowa canu ncodetsa, olokani kulowa m'dziko lacolowaca Yehova m'mene cihemaca Yehovacikhalamo, nimukhale naco colowa pakati pa ife; koma musapikisana ndi Yehova kapena kupikisana nafe, ndi kudzimangira nokha guwa la nsembe, pamodzi ndi guwa la nsembe la Yehova Mulungu wathu.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 22