Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 19:40-51 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

40. Maere acisanu ndi ciwiri anaturukira pfuko la ana a Dani, monga mwa mabanja ao.

41. Ndipo malire a colowa cao anali Zora, ndi Esitaoli ndi Iri-semesi;

42. Saalabini, ndi Aijaloni ndi ltila;

43. ndi Eloni ndi Timna ndi Ekroni;

44. ndi Eliteke, ndi Gibetoni, ndi Baalati;

45. ndi Yehudi, ndi Bene-beraki, ndi Gatirimoni;

46. ndi Me-jarikoni, ndi Rakoni, ndi malire pandunji pajapo.

47. Koma malire a ana a Dani anaturuka kupitirira iwowa; pakuti ana a Dani anakwera nathira nkhondo ku Lesemu, naulanda naukantha ndi lupanga lakuthwa, naulandira, nakhala m'mwemo, naucha Lesemu, Dani; ndilo dzina la Dani atate wao.

48. Ici ndi colowa ca pfuko la ana a Dani, monga mwa mabanja ao, midzi iyi ndi miraga yao.

49. Ndipo atatha kuligawa dziko likhale colowa cao monga mwa malire ace, ana a Israyeli anapatsa Yoswa mwana wa Nuni colowa pakati pao;

50. monga mwa lamulo la Yehova anampatsa mudzi umene anawapempha, ndiwo Timinatisera, ku mapiri a Efraimu; ndipo anamangamudziwonakhala m'mwemo.

51. Izi ndizo zolowa anazigawa Eleazare wansembe, ndi Yoswa mwana wa Nuni, ndi akulu a nyumba za atate a mapfuko a ana a Israyeli, zikhale zao zao, ndi kulota maere ku Silo pamaso pa Yehova ku khomo la cihema cokomanako. Momwemo anatha kuligawa dziko.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 19