Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 18:6-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo muzilemba dziko likhale magawo asanu ndi awiri, ndi kubwera nao kuno kwa ine malembo ace; ndipo ndidzakuloterani maere pane pamaso pa Yehova Mulungu wathu.

7. Pakuti Alevi alibe gawo pakati pa inu; pakuti unsembe wa Yehova ndiwo colowa cao. Koma Gadi, ndi Rubeni, ndi pfuko la Manase logawika pakati adalandira colowa cao tsidya lija la Yordano kum'mawa, cimene Mose mtumiki wa Yehova adawapatsa.

8. Ndipo amunawo ananyamuka, namuka; ndipo Yoswa analamulira opita kulemba dzikowo, ndi kuti, Mukani, muyendeyende pakati pa dziko, ndi kulilemba, oimubwerenso kwa ine, ndipo ndidzakuloterani maere pane pamaso pa Yehova pa Silo.

9. Namuka amunawo, napitapita pakati pa dziko, nalilemba m'buku, nayesa midzi yace, magawo asanu, nabwera kwa Yoswa ku cigono ku Silo.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 18