Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 18:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo msonkhano wonse wa ana a Israyeli unasonkhana ku Silo, nuutsa komweko cihema cokomanako; ndipo dziko linawagoniera.

2. Ndipo anatsala mwa ana a Israyeli mapfuko asanu ndi awiri osawagawira colowa cao.

3. Ndipo Yoswa anati kwa ana a Israyeli, Mucedwa mpaka liti kulowa ndi kulandira dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu anakupatsani?

4. Mudzifunire amuna, pfuko liri lonse amuna atatu; kuti ndiwatume, anyamuke, nayendeyende iwo pakati pa dziko, nalilembe monga mwa colowa cao; nabwereoso kwa ine.

5. Ndipo adzaligawa magawo asanu ndi awiri; Yuda adzakhala m'malire ace kumwela, ndi a m'nyumba ya Yosefe adzakhala m'malire mwao kumpoto.

6. Ndipo muzilemba dziko likhale magawo asanu ndi awiri, ndi kubwera nao kuno kwa ine malembo ace; ndipo ndidzakuloterani maere pane pamaso pa Yehova Mulungu wathu.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 18