Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 17:5-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo anamgwera Manase magawo khumi, osawerenga dziko la Gileadi ndi Basana lokhala tsidya lija la Yordano:

6. popeza ana akazi a Manase adalandira colowa pakati pa ana ace amuna; ndi dziko la Gileadi linakhala la ana a Manase otsala.

7. Ndipo malire a Manase anayambira ku Aseri, kumka ku Mika-metatu, wokhala cakuno ca Sekemu; namuka malire ku dzanja lamanja kwa nzika za Enitapua.

8. Dziko la Tapua linali la Manase; koma Tapua mpaka malire a Manase linakhala la ana a Efraimu.

9. Natsikira malire ku mtsinje wa Kana, kumwera kwa mtsinje; midzi iyi inakhala ya Efraimu pakati pa midzi ya Manase; ndi malire a Manase anali kumpoto kwa mtsinje; ndimaturukiro ace anali kunyanja;

10. kumwera nkwa Efraimu ndi kumpoto nkwa Manase, ndi malire ace ndi nyanja; ndi kumpoto anakomana ndi Aseri, ndi kum'mawa anakomana ndi Isakara.

11. Ndipo m'Isakara ndi m'Aseri Manase anali nao Betiseani ndi midzi yace, ndi Ibleamu ndi midzi yace, ndi nzika za Doro ndi midzi yace, ndi nzika za Eni-doro ndi midzi yace, ndi nzika za Taanaki ndi midzi yace, ndi nzika za Megido ndi midzi yace; dziko la mapiri atatu.

12. Koma ana a Manase sanatha kuingitsa a m'midzi aja, popeza Akananjanafuna kukhala m'dziko lija.

13. Ndipo kunali pamene ana a lsrayeli atakula mphamvu anasonkhetsa Akanani osawaingitsa onse.

14. Pamenepo ana a Yosefe ananena ndi Yoswa, ndi kuti, Watipatsiranji colowa cathu camaere cimodzi ndi gawo limodzi, popeza ife ndife anthu aunyinji, pakuti Yehova anatidalitsa ndi pano pomwe?

Werengani mutu wathunthu Yoswa 17