Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 16:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo gawo La ana a Yosefe linaturuka kucokera ku Yordano ku Yeriko, ku madzi a Yeriko kum'mawa, kucipululu, nakwera kucokera ku Yeriko kumka kumapiri ku Beteli;

2. naturuka ku Beteli kumka ku Luzi, napitirira kumka ku malire a Aariki, ku Atarotu;

3. natsikira kumadzulo kumka ku malire a Ayafeleti, ku malire a Beti-horoni wa kunsi, ndi ku Gezeri; ndi maturukiro ace anali kunyanja.

4. Motero ana a Yosefe, Manase ndi Efraimu analandira colowa cao,

Werengani mutu wathunthu Yoswa 16