Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yona 4:5-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Pamenepo Yona anaturuka m'mudzi, nakhala pansi kum'mawa kwa mudzi, nadzimangira komweko thandala, nakhala pansi pace mumthunzi mpaka adzaona cocitikira mudzi.

6. Ndipo Yehova Mulungu anaikiratu msatsi, naumeretsera Yona, ucite mthunzi pamutu pace, kumlanditsa m'nsautso yace. Ndipo Yona anakondwera kwambiri cifukwa ca msatsiwo.

7. Koma Mulungu anauikira mphanzi pakuca m'mawa mwace, ndiyo inadya msatsi, nufota.

8. Ndipo kunali, poturuka dzuwa Mulungu anaika mphepo ya kum'mawa yotentha, ndipo dzuwa linatentha mutu wace wa Yona, nalefuka iye, nadzipempherera kuti afe; nati, Kundikomera ine kufa, kukhala ndi moyo ai.

9. Ndipo Mulungu anati kwa Yona, Uyenera kodi kupsa mtima cifukwa ca msatsiwo? Nati iye, Ee, kundiyenera ine kupsa mtima mpaka imfa.

10. Ndipo Yehova anati, Unacitira cifundo msatsiwo umene sunagwirapo nchito, kapena kuumeretsa, umene unamera usiku, nutha usiku;

Werengani mutu wathunthu Yona 4