Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 9:10-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Njerwa zagwa, koma ife tidzamanga ndi miyala yosema; mikuyu yagwetsedwa, koma tidzaisinthanitsa ndi mikungudza.

11. Cifukwa cace Yehova adzamkwezera Rezini olimbana naye, nautsa adani ace;

12. Aramu patsogolo ndi Afilisti pambuyo; ndipo iwo adzadya Israyeli ndi kukamwa koyasama. Mwa izi zonse mkwiyo wace sunacoke, koma dzanja lace liri citambasulire.

13. Koma anthu sanatembenukire kwa Iye amene anawamenya, ngakhale kufuna Yehova wa makamu.

14. Cifukwa cace Yehova adzadula mutu wa Israyeli ndi mcira wace; nthambi ya kanjedza ndi mlulu, tsiku limodzi.

15. Nkhalamba ndi wolemekezeka ndiye mutu, ndi mneneri wophunzitsa zonama ndiye mcira.

16. Pakuti iwo amene atsogolera anthuwa, ndiwo awasokeretsa; ndipo iwo amene atsogoleredwa nao aonongeka.

17. Cifukwa cace Ambuye sadzakondwera ndi anyamata ao, ngakhale kuwacitira cifundo amasiye ao ana ndi akazi; popeza yense ali wodetsa ndi wocimwa, m'kamwa monse mulankhula zopusa. Mwa izi zonse mkwiyo wace sunacoke, koma dzanja lace liri citambasulire.

18. Pakuti kucimwa kwayaka ngati moto kumariza lunguzi ndi minga, inde kuyaka m'nkhalango ya m'thengo, ndipo zifuka capamwamba, m'mitambo yautsi yocindikira.

19. M'kukwiya kwa Yehova wa makamu, dziko latenthedwa ndithu, anthunso ali ngati nkhuni; palibe munthu wocitira mbale wace cisoni.

20. Ndipo wina adzakwatula ndi dzanja lamanja, nakhala ndi njala; ndipo adzadya ndi dzanja lamanzere, osakhutai; iwo adzadya munthu yense nyama ya mkono wace wa iye mwini.

21. Manase adzadya Efraimu ndi Efraimu adzadya Manase, ndipo iwo pamodzi adzadyana ndi Yuda. Mwa izi zonse mkwiyo wace sunacoke, koma dzanja lace liri citambasulire.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 9