Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 7:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo panali masiku a Ahazi, mwana wa Yotamu, mwana wa Uziya, mfumu ya Yuda, kuti Rezini, mfumu ya Aramu, ndi Peka, mwana wa Remaliya, mfumu ya Israyeli, anakwera kunka ku Yerusalemu, kumenyana nao; koma sanathe kuupamnana.

2. Ndipo anauza a nyumba ya Davide, kuti Aramu wapangana ndi Efraimu. Ndipo mtima wace unagwedezeka, ndi mtima wa anthu ace, monga mitengo ya m'nkhalango igwedezeka ndi mphepo.

3. Ndipo Yehova anati kwa Yesaya, Turuka tsopano kukacingamira Ahazi, iwe ndi Seariyasubu, mwana wamwamuna wako, pa mamariziro a mcerenje wa thamanda la pamtunda, ku khwalala la pa mwaniko wa wotsuka nsaru;

4. nukati kwa iye, Cenjera, khala ulipo; usaope, mtima wako usalefuke, cifukwa ca zidutswa ziwirizi za miuni yofuka, cifukwa ca mkwiyo waukali wa Rezini ndi Aramu, ndi wa mwana wa Remaliya.

5. Cifukwa Aramu ndi Efraimu, ndi mwana wa Remaliya anapangana kukucitira zoipa, nati,

6. Tiyeni, tikwere, timenyane ndi Yuda, timbvute; tiyeni, tidzigumulire mpata, pamenepo tikhazike mfumu pakati pace, ngakhale mwana wamwamuna wa Tabeeli;

7. atero Ambuye Yehova, Upo wao sudzaimai, sudzacitidwa.

8. Pakuti mutu wa Aramu ndi Damasiko, ndi mutu wa Damasiko ndi Rezini, zisadapite zaka makumi asanu ndi limodzi mphambu zisanu Efraimu adzatyokatyoka, sadzakhalanso mtundu wa anthu;

9. ndipo mutu wa Efraimu ndi Samariya, ndi mutu wa Samariya ndi mwana wa Remaliya, mukapanda kukhulupirira ndithu simudzakhazikika.

10. Ndipo Yehova ananenanso kwa Ahazi nati,

Werengani mutu wathunthu Yesaya 7