Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 65:19-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ndipo ndidzasangalala m'Yerusalemu, ndi kukondwera mwa anthu anga; ndipo mau akulira sadzamvekanso mwa iye, pena mau akupfuula.

20. Sipadzakhalanso khanda la masiku, pena munthu wokalamba osakwanitsa masiku ace; pakuti mwana adzafa wa zaka zana limodzi; ndipo wocimwa pokhala wa zaka zana limodzi adzatembereredwa.

21. Ndipo iwo adzamanga nyumba ndi kukhalamo; ndipo iwo adzanka minda yamphesa, ndi kudya zipatso zace.

22. Iwo sadzamanga, ndi wina kukhalamo; iwo sadzanka, ndi wina kudya; pakuti monga masiku a mtengo adzakhalamasiku a anthu anga; ndi osankhidwa anga adzasangalala nthawi zambiri ndi nchito za manja ao.

23. Iwo sadzagwira nchito mwacabe, pena kubalira tsoka; pakuti iwo ndiwo mbeu ya odalitsidwa a Yehova, ndi obadwa ao adzakhala pamodzi ndi iwo.

24. Ndipo padzakhala kuti iwo asanaitane Ine, ndidzayankha; ndipo ali cilankhulire, Ine ndidzamva.

25. Mmbulu ndi mwana wa nkhosa zidzadyera pamodzi; ndi mkango udzadya udzu ngati ng'ombe; ndi pfumbi lidzakhala cakudya ca njoka; sizidzapwetekana, kapena kusakazana m'phiri langa lonse lopatulika, ati Yehova.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 65