Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 54:2-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Kuza malo a hema wako, afunyulule zinsaru za mokhalamo iwe; usaleke, tanimphitsa zingwe zako, limbitsa zikhomo zako.

3. Pakuti iwe udzafalikira ponse pa dzanja lamanja ndi lamanzere, ndipo mbeu yako idzalandira amitundu colowa cao, ndi kukhalitsa anthu m'mabwinja.

4. Usaope, pakuti sudzakhala ndi manyazi; usasokonezedwe, pakuti sudzacitidwa manyazi; pakuti udzaiwala manyazi a ubwana wako, ndi citonzo ca umasiye wako sudzacikumbukiranso.

5. Pakuti Mlengi wako ndiye mwamuna wako; Yehova wa makamu ndiye dzina lace; ndi Woyera wa Israyeli ndiye Mombolo wako; Iye adzachedwa Mulungu wa dziko lonse lapansi.

6. Pakuti Yehova wakuitana iwe monga mkazi wakusiyidwa ndi wosauka m'mzimu, ngakhale mkazi wa ubwana wocotsedwa, ati Mulungu wako.

7. Kamphindi kakang'ono ndakusiya iwe, koma ndi cifundo cambiri ndidzakusonkhanitsa.

8. M'kukwiya kwa kusefukira ndinakubisira nkhope yanga kamphindi; koma ndi kukoma mtima kwa cikhalire ndidzakucitira cifundo, ati Yehova Mombolo wako.

9. Pakuti kumeneku kuli kwa Ine monga madzi a Nowa; pakuti monga ndinalumbira kuti madzi a Nowa sadzamizanso pa dziko lapansi, momwemo ndinalumbira kuti sindidzakukwiyira iwe, pena kukudzudzula.

10. Pakuti mapiri adzacoka, ndi zitunda zidzasunthika; koma kukoma mtima kwanga sikudzakucokera iwe, kapena kusunthika cipangano canga ca mtendere, ati Yehova amene wakucitira iwe cifundo.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 54