Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 52:3-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Pakuti atero Yehova, Inu munagulitsidwa cabe, ndipo mudzaomboledwa opanda ndalama.

4. Pakuti Ambuye Yehova atero, Anthu anga ananka ku Aigupto poyamba paja, kukakhala kumeneko; ndipo Asuri anawatsendereza popanda cifukwa.

5. Cifukwa cace kodi ndicitenji pano? ati Yehova; popeza anthu anga acotsedwa popanda kanthu? akuwalamulira awaliritsa, ati Yehova; ndipo dzina langa licitidwa mwano tsiku lonse kosalekeza.

6. Cifukwa cace anthu anga adzadziwa dzina langa; cifukwa cacersiku limenelo iwo adzadziwa kuti Ine ndine amene ndinena; taonani, ndine pano.

7. Ha, akongolatu pamapiri mapazi a iye amene adza ndi uthenga wabwino, amene abukitsa mtendere, amene adza ndi uthenga wabwino wa zinthu zabwino, amene abukitsa cipulumutso; amene ati kwa Ziyoni, Mulungu wako ndi mfumu.

8. Mau a alonda ako! akweza mau, ayimba pamodzi; pakuti adzaona maso ndi maso, pamene Yehova abwerera kudza ku Ziyoni.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 52