Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 52:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Galamuka galamuka, tabvala mphamvu zako, Ziyoni; tabvala zobvala zako zokongola, Yerusalemu, mzinda wopatulika; pakuti kuyambira tsopano sadzalowanso kwa iwe wosadulidwa ndi wodetsedwa.

2. Dzisanse pfumbi; uka, khala tsonga, Yerusalemu; udzimasulire maunyolo a pakhosi pako, iwe mwana wamkazi wam'nsinga wa Ziyoni.

3. Pakuti atero Yehova, Inu munagulitsidwa cabe, ndipo mudzaomboledwa opanda ndalama.

4. Pakuti Ambuye Yehova atero, Anthu anga ananka ku Aigupto poyamba paja, kukakhala kumeneko; ndipo Asuri anawatsendereza popanda cifukwa.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 52