Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 49:11-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo ndidzasandutsa mapiri anga onse akhale njira, ndipo makwalala anga adzakwezeka.

12. Taonani, awa adzacokera kutari; ndipo taonani, awa ocokera kumpoto, ndi kumadzulo; ndi awa ocokera ku dziko la Sinimu.

13. Yimbani inu, m'mwamba, nukondwere iwe dziko lapansi, yimbani inu mapiri, pakuti Yehova watonthoza mtima wa anthu ace, nadzacitira cifundo obvutidwa ace.

14. Koma Ziyoni anati, Yehova wandisiya ine, ndipo Ambuye wandiiwala ine.

15. Kodi mkazi angaiwale mwana wace wa pabere, kuti iye sangacitire cifundo mwana wombala iye? inde awa angaiwale, koma Ine sindingaiwale iwe.

16. Taona ndakulembera iwe pa zikhato za manja anga; makoma ako alipo masiku onse pamaso panga,

17. Ana ako afulumira; opasula ako ndi iwo amene anakusakaza adzacoka pa iwe.

18. Tukula maso ako kuunguza-unguza, nuone; onsewa asonkhana pamodzi, nadza kwa iwe. Pali Ine, ati Yehova, iwe ndithu udzadzibveka wekha ndi iwo onse, monga ndi cokometsera, ndi kudzimangira nao m'cuuno ngati mkwatibwi.

19. Pakuti, kunena za tnalo ako osiyidwa ndi abwinja ndi dziko lako limene lapasulidwa tsopano, ndithu iwe udzakhala wocepera okhalamo, ndi iwo amene anakumeza iwe adzakhala kutari.

20. Ana ako amasiye adzanena m'makutu ako, Malo andicepera ine, ndipatse malo, kuti ndikhalemo.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 49