Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 45:15-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndithu Inu ndinu Mulungu, amene mudzibisa nokha, Mulungu wa Israyeli, Mpulumutsi.

16. Iwo adzakhala ndi manyazi, inde, adzathedwa nzeru onsewo; adzalowa m'masokonezo pamodzi, amene apanga mafano.

17. Koma Israyeli adzapulumutsidwa ndi Yehova ndi cipulumutso cosatha; inu simudzakhala ndi manyazi, pena kuthedwa nzeru ku nthawi zosatha.

18. Pakuti atero Yehova amene analenga kumwamba, Iye ndiye Mulungu amene anaumba dziko lapansi, nalipanga; Iye analikhazikitsa, sanalilenga mwacabe; Iye analiumba akhalemo anthu; Ine ndine Yehova; ndipo palibenso wina.

19. Ine sindinanena m'tseri m'malo a dziko la mdima; Ine sindinati kwa mbeu ya Yakobo, Mundifune Ine mwacabe; Ine Yehova ndinena cilungamo, ndinena zimene ziri zoona.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 45