Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 44:16-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Iye atenthako mbali yina pamoto; ndi mbali yinayo adya nyama; akazinga zokazinga, nakhuta, inde, aotha moto, nati, Ha, ndakongonoka, ndauona moto.

17. Ndipo cotsalaco apanga mlungu, ngakhale fano lace losema; iye aligwadira, nalipembedza, nalipemphera nati, Ndipulumutse ine, cifukwa kuti ndinu mulungu wanga.

18. Iwo sadziwa, kapena kuzindikira, cifukwa pamaso pao papakidwa thope, kuti sangaone, ndi m'mitima mwao kuti sangadziwitse.

19. Palibe wina wokumbukira, kapena kudziwa, kapena kuzindikira, ndi kuti, Ndatentha mbali yina pamoto, inde ndaocanso mkate pamakala pace, ndakazinga nyama ndi kuidya; kodi ndicipange cotsala cace, cikhale conyansa? ndidzagwadira kodi tsinde la mtengo?

20. Iye adya phulusa; mtima wodzinyenga wampambutsa, kuti iye sangapulumutse moyo wace, pena kunena, Kodi simuli kunama m'dzanja langa lamanja?

21. Kumbukira zinthu izi, Yakobo; ndi Israyeli, pakuti iwe ndiwe mtumiki wanga; ndakuumba, iwe ndiwe mtumiki wanga, Israyeli, sindidzakuiwala.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 44