Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 44:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Koma tsopano, imva Yakobo, mtumiki wanga, ndi Israyeli, amene ndakusankha;

2. atero Yehova, amene anakutenga iwe, nakuumba kucokera m'mimba, amene adzathangata iwe. Usaope Yakobo, mtumiki wanga ndi iwe, Yesuruni, amene ndakusankha iwe.

3. Pakuti ndidzathira madzi pa dziko limene liribe madzi, ndi mitsinje pa nthaka youma; ndidzathira mzimu wanga pa mbeu yako, ndi mdalitso wanga pa obadwa ako;

4. ndipo iwo adzaphuka pakati pa maudzu, ngati msondodzi m'mphepete mwa madzi.

5. Wina adzati, Ine ndiri wa Yehova; ndi wina adzadzicha yekha ndi dzina la Yakobo, ndipo wina adzalemba ndi dzanja lace, Ndine wa Yehova, ndi kudzicha yekha ndi mfunda wa lsrayeli.

6. Atero Yehova, Mfumu ya Israyeli ndi Mombolo wace, Yehova wa makamu, Ine ndiri woyamba ndi womariza, ndi popanda Ine palibenso Mulungu.

7. Ndipo ndani adzaitana monga Ine, ndi kulalikira ici ndi kundilongosolera ici, cikhazikitsire Ine anthu akale? milunguyo iwadziwitse zomwe zirinkudza, ndi za m'tsogolo.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 44