Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 43:14-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Atero Yehova, Mombolo wanu, Woyera wa Israyeli: Cifukwa ca inu ndatumiza ku Babulo, ndipo ndidzatsitsira iwo onse monga othawa, ngakhale Akasidi m'ngalawa za kukondwa kwao.

15. Ine ndine Yehova Woyera wanu, Mlengi wa Israyeli, Mfumu yanu,

16. Atero Yehova, amene akonza njira panyanja, ndi popita m'madzi amphamvu;

17. amene aturutsa gareta ndi ka valo, nkhondo ndi mphamvu; iwo agona pansi pamodzi sadzaukai; iwo atha, azimidwa ngati lawi.

18. Musakumbukire zidapitazo, ngakhale kulingalira zinthu zakale.

19. Taonani, ine ndidzacita cinthu catsopano; tsopano cidzaoneka; kodi simudzacidziwa? Ndidzakonzadi njira m'cipululu, ndi mitsinje m'zidalala.

20. Nyama za m'thengo zidzandilemekeza, ankhandwe ndi nthiwatiwa; cifukwa ndipatsa madzi m'cipululu, ndi mitsinje m'mkhwangwala, ndimwetse anthu anga osankhika;

21. anthu amene ndinadzilengera ndekha, kuti aonetse matamando anga.

22. Komabe iwe sunandiitane Ine, Yakobo; koma iwe walema ndi Ine, Israyeli.

23. Iwe sunanditengere Ine zoweta zazing'ono za nsembe zopsereza zako; kapena kundilemekeza ndi nsembe zako. Sindinakutumikiritsa ndi nsembe zaufa, kapena kukutopetsa ndi zonunkhira.

24. Iwe sunandigulire Ine nzimbe ndi ndarama, pena kundikhutitsa ndi mafuta a nsembe zako. Koma iwe wanditumikiritsa ndi macimo ako, wanditopetsa ndi mphulupulu zako.

25. Ine, Inedi, ndine amene ndifafaniza zolakwa zako, cifukwa ca Ine mwini; ndipo Ine sindidzakumbukira macimo ako.

26. Undikumbutse Ine; tiyeni, tinenane pamodzi; fotokoza mlandu wako, kuti ukalungamitsidwe.

27. Atate wako woyamba anacimwa, ndi otanthauzira ako andilakwira Ine.

28. Cifukwa cace ndidzaipitsa akuru a kacisi, ndipo ndidzasanduliza Yakobo akhale temberero, ndi Israyeli akhale citonzo.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 43