Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 41:24-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Taonani, inu muli acabe, ndi nchito yanu yacabe; wonyansa ali iye amene asankha inu.

25. Ndautsa wina wakucokera kumpoto; ndipo iye wafika wakucokera poturuka dzuwa, amene achula dzina langa; ndipo iye adzafika pa olamulira, monga matope, ndi monga muumbi aponda dothi la mbiya.

26. Ndani wachula ico ciyambire, kuti ife ticidziwe? ndi nthawi zakale, kuti ife tinene, Iye ali wolungama? inde, palibe wina amene achula, inde, palibe wina amene asonyeza, inde, palibe wina amene amvetsa mau anu.

27. Poyamba Ine ndidzati kwa Ziyoni, Taona, taona iwo; ndipo ndidzapereka kwa Yerusalemu wina, amene adza ndi mau abwino.

28. Ndipo pamene ndayang'ana, palibe munthu; ngakhale mwa iwo, palibe phungu, amene angathe kuyankha mau, pamene ndiwafunsa.

29. Taona, iwo onse, nchito zao zikhala zopanda pace ndi zacabe; mafano ao osungunula ndiwo mphepo ndi masokonezo.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 41