Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 30:7-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Pakuti thangata la Aigupto liri lacabe, lopanda pace; cifukwa cace ndamucha wonyada, wokhala cabe.

8. Tsopano pita, ukalembe mauwa pamaso pao pathabwa, nuwalembe m'buku, kuti akakhalebe ku nthawi yam'tsogolo, mboni ya masiku onse.

9. Pakuti ali anthu opanduka, ana onama, ana osafuna kumva cilamulo ca Yehova;

10. amene amati kwa alauli, Mtima wanu usapenye; ndi kwa aneneri, Musanenere kwa ife zinthu zoona, munene kwa ife zinthu zamyadi, munenere zonyenga;

11. cokani inu munjira, patukani m'bande, tiletsereni Woyera wa Israyeli pamaso pathu.

12. Cifukwa cace atero Woyera wa Israyeli, Popeza inu mwanyoza mau awa, nimukhulupirira nsautso ndi mphulupulu, ndi kukhala m'menemo;

13. cifukwa cace kuipa kumeneku kudzakhala kwa inu monga pogumuka pofuna kugwa, monga potukuka m'khoma lalitari, kugumuka kwace kufika modzidzimutsa dzidzidzi.

14. Ndipo Iye adzagumulapo, monga mbiya ya woumba isweka, ndi kuiswaiswa osaileka; ndipo sipadzapezedwa m'zigamphu zace phale lopalira moto pacoso, ngakhale lotungira madzi padziwe.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 30