Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 30:3-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Cifukwa cace mphamvu za Farao zidzakhala kwa inu manyazi, ndi kukhulupirira mthunzi wa Aigupto kudzakhala cisokonezo canu.

4. Pakuti akalonga ace ali pa Zaani, ndi mithenga yace yafika ku Hanesi.

5. Iwo onse adzakhala ndi manyazi, ndi anthu amene sangapindule nao kanthu, amene sakhala kwa iwo thangata, pena phindu, koma manyazi ndi citonzo.

6. Katundu wa zirombo za kumwera.M'dziko lobvuta ndi lopweteka, kumeneko kucokera mkango waukazi, ndi wamphongo, mphiri, ndi njoka youluka yamoto, iwo anyamula cuma cao pamsana pa aburu, ndi ang'ono zolemera zao pa malinundu a ngamila, kunka kwa anthu amene sadzapindula nao.

7. Pakuti thangata la Aigupto liri lacabe, lopanda pace; cifukwa cace ndamucha wonyada, wokhala cabe.

8. Tsopano pita, ukalembe mauwa pamaso pao pathabwa, nuwalembe m'buku, kuti akakhalebe ku nthawi yam'tsogolo, mboni ya masiku onse.

9. Pakuti ali anthu opanduka, ana onama, ana osafuna kumva cilamulo ca Yehova;

10. amene amati kwa alauli, Mtima wanu usapenye; ndi kwa aneneri, Musanenere kwa ife zinthu zoona, munene kwa ife zinthu zamyadi, munenere zonyenga;

11. cokani inu munjira, patukani m'bande, tiletsereni Woyera wa Israyeli pamaso pathu.

12. Cifukwa cace atero Woyera wa Israyeli, Popeza inu mwanyoza mau awa, nimukhulupirira nsautso ndi mphulupulu, ndi kukhala m'menemo;

13. cifukwa cace kuipa kumeneku kudzakhala kwa inu monga pogumuka pofuna kugwa, monga potukuka m'khoma lalitari, kugumuka kwace kufika modzidzimutsa dzidzidzi.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 30