Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 25:4-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Cifukwa Inu mwakhala linga la aumphawi, linga la osowa m'kubvutidwa kwace, pobisalira cimphepo, mthunzi wa pa dzuwa, pamene kuomba kwa akuopsya kufanana ndi cimphepo cakuomba chemba.

5. Monga kutentha m'malo ouma, Inu mudzaletsa phokoso la alendo; nyimbo ya akuopsya idzaletseka, monga mthunzi uletsa dzuwa.

6. Ndipo m'phiri limendi Yehova wa makamu adzakonzera anthu ace onse phwando la zinthu zonona, phwando la vinyo wa pamitsokwe, la zinthu zonona za mafuta okha okha, la vinyo wansenga wokuntha bwino.

7. Ndipo Iye adzaononga m'phiri limeneli cophimba nkhope cobvundikira mitundu yonse ya anthu, ndi nsaru yokuta amitundu onse.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 25