Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 24:7-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Vinyo watsopano alira, mpesa ulefuka, mitima yonse yokondwa iusa moyo.

8. Kusangalala kwa mangaka kwalekeka, phokoso la iwo amene aserera litha, kukondwa kwa mngoli kwalekeka.

9. Iwo sadzamwa vinyo ndi kuyimba nyimbo; cakumwa caukali cidzawawa kwa iwo amene acimwa.

10. Mudzi wosokonezeka wagwetsedwa pansi; nyumba zonse zatsekedwa, kuti asalowemo munthu.

11. Muli mpfuu m'makwalala cifukwa ca vinyo; kukondwa konse kwadetsedwa, kusangalala kwa dziko kwatha.

12. M'mudzi mwatsala bwinja, ndi cipata camenyedwa ndi cipasuko.

13. Cifukwa cace padzakhala cotero pakati pa dziko mwa anthu, ngati kugwedeza kwa mtengo waazitona, ngati khunkha la mphesa, pakutha masika ace.

14. Amenewa adzakweza mau ao, nadzapfuula; cifukwa ca cifumu ca Yehova, iwo adzapfuula zolimba panyanja.

15. Cifukwa cace lemekezani inu Yehova kum'mawa, ngakhale dzina la Yehova, Mulungu wa Israyeli, m'zisumbu za m'nyanja.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 24