Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 15:6-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Pakuti pa madzi a Nimirimi padzakhala mabwinja; papeza udzu wafota, msipu watha.

7. Cifukwa cace zocuruka adazipeza, ndi zosungidwa zao adzazitenga kunka nazo ku mtsinje wa mabango.

8. Pakuti kulira kwamveka kuzungulira malire a Moabu; kukuwa kwace kwafikira ku Eglaimu, ndi kukuwa kwace kwafikira ku Beerelimu.

9. Pakuti madzi a Dimoni adzala mwazi; pakuti ndidzatengera zina pa! Dimoni, mkango pa iye amene anapulumuka ku Moabu, ndi pa otsala am'dziko.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 15